1. Pfuulirani kwa Mulungu, dziko lonse lapansi.
2. Yimbirani ulemerero wa dzina lace;Pomlemekeza mumcitire ulemerero.
3. Nenani kwa Mulungu, Ha, nchito zanu nzoopsa nanga!Cifukwa ca mphamvu yanu yaikuru adani anu adzagonjera Inu,
4. Dziko lonse lapansi lidzakugwadirani,Ndipo lidzakuyimbirani;Adzayimbira dzina lanu.
5. Idzani, muone nchito za Mulungu;Zocitira Iye ana a anthu nzoopsa.
6. Anasanduliza nyanja ikhale mtunda:Anaoloka mtsinje coponda pansi:Apo tinakondwera mwa Iye.
7. Acita ufumu mwa mphamvu yace kosatha;Maso ace ayang'anira amitundu;Opikisana ndi Iye asadzikuze.
8. Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu,Ndipo mumveketse liu la cilemekezo cace: