8. Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;Onse akuwaona adzawathawa.
9. Ndipo anthu onse adzacita mantha;Nadzabukitsa cocita Mulungu,Nadzasamalira nchito yace.
10. Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye;Ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.