10. Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama cifwamba;Cikacuruka cuma musakhazikepo mitima yanu.
11. Mulungu ananena kamodzi, ndinacimva kawiri:Kuti mphamvu ndi yace ya Mulungu:
12. Cifundonso ndi canu, Ambuye:Cifukwa Inu musudzula munthu ali yense monga mwa nchito yace.