1. Kodi muli cete ndithu poyenera inu kunena zolungama?Muweruza ana a anthu molunjika kodi?
2. Inde, mumtima mucita zosalungama;Pa dziko lapansi mugawira anthu ciwawa ca m'manja mwanu.
3. Oipa acita cilendo cibadwire:Asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.