11. M'kati mwace muli kusakaza:Ciwawa ndi cinyengo sizicoka m'makwalala ace.
12. Pakuti si mdani amene ananditonzayo;Pakadatero ndikadacilola:Amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida;Pakadatero ndikadambisalira:
13. Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane,Tsamwali wanga, wodziwana nane.
14. Tinapangirana upo wokoma,Tinaperekeza khamu la anthu popita ku nyumba ya Mulungu.
15. Imfa iwagwere modzidzimutsa,Atsikire kumanda ali amoyo:Pakuti m'mokhala mwao muli zoipa pakati pao,
16. Koma ine ndidzapfuulira kwa Mulungu;Ndipo Yehova atizandipulumutsa.
17. Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula,Ndipo adzamva mau anga.
18. Anaombola moyo wanga ku nkhondo yondilaka, ndikhale mumtendere:Pakuti ndiwo ambiri okangana nane.
19. Mulungu adzamva, nadzawasautsa,Ndiye wokhalabe ciyambire kale lomwe.Popeza iwowa sasinthika konse,Ndipo saopa Mulungu.
20. Anaturutsa manja ace awagwire iwo akuyanjana naye:Anaipsa pangano lace.
21. Pakamwa pace mposalala ngati mafuta amkaka,Koma mumtima mwace munali nkhondo:Mau ace ngofewa ngati mafuta oyenga,Koma anali malupanga osololasolola.
22. Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iyeadzakugwiriziza:Nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.
23. Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira ku dzenje la cionongeko:Anthu okhetsa mwazi ndi acinyengo masiku ao sadzafikira nusu;Koma ine ndidzakhulupirira Inu.