1. Mtima wanga usefukira naco cinthu cokoma:Ndinena zopeka ine za mfumu:Lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.
2. Inu ndinu wokongola ndithu kuposa ana a anthu;Anakutsanulirani cisomo pa milomo yanu:Cifukwa cace Mulungu anakudalitsani kosatha.
3. Dzimangireni lupanga lanu m'cuuno mwanu, wamphamvu inu,Ndi ulemerero wanu ndi ukulu wanu.