9. Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala cifukwa ninji?Ndimayenderanji wakulira Cifukwa ca kundipsinja mdaniyo?
10. Adani anga andinyoza ndi kundityola mafupa anga;Pakunena ndine dzuwa lonse,Mulungu wako ali kuti?
11. Udziweramiranji moyo wanga iwe?Ndi kuzingwa m'kati mwanga?Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso,Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga ndi Mulungu wanga,