7. Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira ciani?Ciyembekezo canga ciri pa Inu.
8. Ndipulumutseni kwa zolakwa zangazonse:Musandiike ndikhale cotonza ca wopusa.
9. Ndinakhala du, sindinatsegula pakamwa panga;Cifukwa inu mudacicita.
10. Mundicotsere cobvutitsa canu;Pandithera ine cifukwa ca kulanga kwa dzanja lanu.
11. Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula cifukwa ca mphulupulu,Mukanganula kukongola kwace monga mumacita ndi kadzoce:Indedi, munthu ali yense ali cabe.
12. Imvani pemphero langa, Yehova, ndipo cherani khutu kulira kwanga;Musakhale cete pa misozi yanga:Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu,Wosakhazikika, monga makolo anga onse.
13. Ndiloleni, kuti nditsitsimuke,Ndisanamuke ndi kukhala kuli zi.