5. Mabala anga anunkha, adaola, Cifukwa ca kupusa kwanga.
6. Ndapindika, ndawerama kwakukuru;Ndimayenda woliralira tsiku lonse.
7. Pakuti m'cuuno mwanga mutentha kwambiri;Palibe pamoyo m'mnofu mwanga,
8. Ndafoka ine, ndipo ndacinjizidwa:Ndabangula cifukwa ca kumyuka mtima wanga.