1. Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu:Ndipo musandilange moopsa m'mtima mwanu.
2. Pakuti mibvi yanu yandilowa,Ndi dzanja lanu landigwera.
3. Mumnofu mwanga mulibe camoyo cifukwa ca ukali wanu;Ndipo m'mafupa anga simuzizira, cifukwa ca colakwa canga.