27. Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.
28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.
29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.
30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.
31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.
32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.
33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.
34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,
35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.
36. Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.
37. Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.
38. Koma olakwa adzaonongeka pamodzi:Matsiriziro a oipa adzadutidwa.
39. Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova,Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.