9. Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.
10. Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka;Nauluka msanga pa mapiko a mphepo,
11. Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga;Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.
12. Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka,Matalala ndi makala amoto.
13. Ndipo anagunda m'mwamba Yehova,Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace;Matalala ndi makala amoto,
14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.
15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.