2. Mlemekezeni, angelo ace onse;Mlemekezeni, makamu ace onse.
3. Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;Mlemekezeni, nyenyezi zonse zaunikira.
4. Mlemekezeni, m'mwambamwamba,Ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.
5. Alemekeze dzina la Yehova;Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.
6. Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi;Anazipatsa cilamulo cosatumphika.
7. Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi,Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;
8. Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu;Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;
9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:
10. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;
11. Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;Zinduna ndi oweruza onse a padziko;
12. Anyamata ndiponso anamwali;Okalamba pamodzi ndi ana:
13. Alemekeze dzina la Yehova;Pakuti dzina lace lokha ndi lokwezeka;Ulemerero wace uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo.