1. Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;Ndisungeni kwa munthu waciwawa;
2. Amene adzipanga zoipa mumtima mwao;Masiku onse amemeza nkhondo.
3. Anola lilime lao ngati njoka;Pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.
4. Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa;Ndisungeni kwa munthu waciwawa;Kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.