8. Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.
9. Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;
10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.
11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:
12. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,Koma usiku uwala ngati usana:Mdima ukunga kuunika.
13. Pakuti Inu munalenga imso zanga;Munandiumba ndisanabadwe ine.
14. Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza;Nchito zanu nzodabwiza;Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.