5. Munandizinga kumbuyo ndi kumaso,Nimunaika dzanja lanu pa ine.
6. Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza:Kundikhalira patali, sindifikirako.
7. Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?
8. Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko;Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.
9. Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca,Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;
10. Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.
11. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku: