1. Yehova, kumbukilani Davide Kuzunzika kwace konse;
2. Kuti analumbira Yehova,Nawindira Wamphamvuyo wa Yakobo, ndi kuti,
3. Ngati ndidzalowa pakhomo pa nyumba yanga,Ngati ndidzakwera pa kama logonapo;
4. Ngati ndidzalola maso anga agone,Kapena zikope zanga ziodzere;
5. Kufikira nditapezera Yehova malo,Cokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?
6. Taonani, tinacimva m'Efrata;Tinacipeza ku cidikha ca kunkhalango.
7. Tidzalowa mokhalamo Iye;Tidzagwadira ku mpando wa mapazi ace.
8. Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu;Inu ndi hema wa mphamvu yanu,