1. Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni,Tinakhala ngati anthu akulota.
2. Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,Ndi lilime lathu linapfuula mokondwera;Pamenepo anati mwa amitundu,Yehova anawacitira iwo zazikuru,
3. Yehova anaticitira ife zazikuru;Potero tikhala okondwera.
4. Bwezani ukapolo wathu, Yehova,Ngati mitsinje ya ku Mwera.
5. Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kupfuula mokondwera.
6. Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;Adzabweranso ndithu ndi kupfuula mokondwera, alikunyamula mitolo yace.
Werengani mutu wathunthu Masalmo 126