22. Mwala umene omangawo anaukanaWakhala mutu wa pangondya.
23. Ici cidzera kwa Yehova;Ncodabwiza ici pamaso pathu.
24. Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;Tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.
25. Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.
26. Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova;Takudalitsani kocokera m'nyumba ya Yehova.