1. Mose ndi Aroni, nati,
2. Nenani nao ana a Israyeli, nimuti nao, Pamene mwamuna ali yense ali ndi nthenda yakukha m'thupi mwace, akhale wodetsedwa, cifukwaca kukha kwace.
3. Ndipo kudetsedwa kwa kukha kwace ndiko: ngakhale cakukhaco cituruka m'thupi mwace, ngakhale caleka m'thupi mwace, ndiko kumdetsa kwace.
4. Kama ali yense agonapo wakukhayo ali wodetsedwa; ndi cinthu ciri conse acikhalira ciri codetsedwa.