14. Ana amuna a Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni, mkazi wace wa Esau, ndi awa: ndipo iye anambalira Esau Jeusi, ndi Jalamu, ndi Kora.
15. Amenewa ndi mafumu a ana amuna a Esau: ana amuna a Elifazi woyamba wa Esau: mfumu Temani, mfumu Omari, mfumu Zefo, mfumu Kenazi,
16. mfumu Kora, mfumu Gatamu, mfumu Amaleki: amenewa ndi mafumu a kwa Elifazi m'dziko la Edomu: amenewa ndi ana amuna a Ada.
17. Amenewa ndi ana amuna a Reueli mwana wamwamuna wa Esau: mfumu Nahati, mfumu Zera, mfumu Sama, mfumu Miza; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Reueli m'dziko la Edomu: amenewa ndi ana amuna a Basemati mkazi wace wa Esau.
18. Amenewa ndi ana amuna a Oholibama mkazi wace wa Esau; mfumu Jeusi, mfumu Jalamu, mfumu Kora, amenewa ndi mafumu obadwa kwa Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mkazi wace wa Esau.
19. Amenewa ndi ana amuna a Esau, amenewa ndi mafumu ao; yemweyo ndi Edomu.
20. Amenewa ndi ana amuna a Seiri Mhori, okhala m'dzikomo: Lotani ndi Sobala, ndi Zibeoni, ndi Ana,
21. ndi Disoni ndi Ezeri ndi Disani; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Ahori, ana a Seiri, m'dziko la Edomu.
22. Ndi ana a Lotani anali Hori ndi Hemamu: mlongo wace wa Lotani anali Timna.
23. Ana a Sobali ndi awa: Alivani ndi Manahati ndi Ebali, Sefo ndi Onamu.
24. Ana a Zibeoni ndi amenewa: Aia ndi Ana; ameneyo ndiye Ana uja anapeza akasupe a madzi amoto m'cipululu, pakudyetsa aburu a Zibeoni atate wace.
25. Ana a Ana ndi awa: Disoni ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana.
26. Ana a Disoni ndi awa: Hemadani ndi Esibani ndi Itirani, ndi Kerana.
27. Ana a Ezeri ndi awa: Biliha, ndi Zavani, ndi Akani.
28. Ana a Disoni ndi awa: Uzi ndi Arana.
29. Mafumu obadwa kwa Ahori: mfumu Lotani, mfumu Sobali, mfumu Zibeoni, mfumu Ana,