1. Mibadwo ya Esau (ndiye Edomu) ndi iyi:
2. Esau anatenga akazi ace a ana akazi a m'Kanani: Ada mwana wamkazi wa Eloni Mhiti, ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni Mhivi;
3. ndi Basemati mwana wamkazi wa lsmayeli, mlongo wace wa Nabayoti.
4. Ndipo Ada anambalira Esau Elifazi; ndipo Basemati anabala Reueli;