1. Ndipo Abrahamu anatenga mkazi wina dzina lace Ketura.
2. Ndipo anambalira iye Zimerani ndi Yokesani ndi Medani, ndi Midyani, ndi Yisebaki, ndi Sua.
3. Ndipo Yokesani anabala Seba, ndi Dedani. Ana a Dedani ndi Aasuri, ndi Aletusi, ndi Aleumi.
4. Ana a Midyani: Efa, ndi Efere, ndi Hanoki, ndi Abida, ndi Elida. Onse amenewa ndi ana a Ketura.
5. Ndipo Abrahamu amwali anampatsa Isake zonse anali nazo.