30. Ndipo Mose anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.
31. Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nacotsera Farao ndi anyamata ace ndi anthu ace mizazayo, sunatsala ndi umodzi wonse.
32. Koma Farao anaumitsa mtima wace nthawi yomweyonso, ndipo sanalola anthu amuke.