11. Ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahalomu.
12. Ndi mzere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama.
13. Ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; inakhala yogwirika ndi golidi maikidwe ace.
14. Ndipo miyalayi inakhala monga mwa maina a ana a Israyeli, khumi ndi awiri, monga mwa maina ao; ngati malocedwe a cosindikizira, yonse monga mwa maina ace, kwa mafuko khumi ndi awiriwo.
15. Ndipo anapangira pacapacifuwa maunyolo ngati zingwe, nchito yopota ya golidi woona.