23. Ukacite cinthuci, ndi Mulungu akakuuza cotero, udzakhoza kupirira, ndi anthu awa onse adzapita kwao mumtendere.
24. Ndipo Mose anamvera mau a mpongozi wace, nacita zonse adazinena.
25. Ndipo Mose anasankha amuna amtima mwa Aisrayeli onse, nawaika akuru a pa anthu, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, ndi akuru a pa makumi.
26. Ndipo anaweruza anthu nthawi zonse; mlandu wakuwalaka amabwera nao kwa Mose, ndi milandu yaing'ono yonse amaweruza okha.
27. Ndipo Mose analola mpongozi wace amuke; ndipo anacoka kumka ku dziko lace.