47. Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;Ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la cipulumutso canga;
48. Inde Mulungu wakundibwezera cilango ine,Ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.
49. Amene anditurutsa kwa adani anga;Inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira;Mundipulumutsa kwa munthu waciwawa.
50. Cifukwa cace ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu,Ndipo ndidzayimba zolemekeza dzina lanu.
51. Iye apatsa mfumu yace cipulumutso cacikuru;Naonetsera cifundo wodzozedwa wace,Kwa Davide ndi mbeu yace ku nthawi zonse.