13. Ceza ca pamaso paceMakala a mota anayaka,
14. Yehova anagunda kumwamba;Ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ace.
15. Ndipo iye anatumiza mibvi, nawawaza;Mphezi, nawaopsa,
16. Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka,Maziko a dziko anaonekera poyera,Ndi mthonzo wa Yehova,Ndi mpumo wa mweya wa m'mphuno mwace.
17. Iye anatumiza kucokera kumwamba nanditenga;Iye ananditurutsa m'madzi akuru;
18. Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,Kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu,
19. Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga,
20. Iye ananditurutsanso ku malo akuru;Iye anandipulumutsa, cifukwa akondwera ndi ine.
21. Yehova anandibwezera monga mwa colungama canga;Monga mwa kuvera kwa manja anga anandipatsa mphotho.
22. Pakuti ndinasunga njira za Yehova,Osapambukira koipa kusiya Mulungu wanga.
23. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga;Ndipo za malemba ace, sindinawapambukira.