Ndipo Abisalomu analawirira, nakaima pa njira ya kucipata; ndipo kunatero, pakakhala munthu ali yense ndi mrandu woyenera kufika kwa mfumu kuti aweruze, Abisalomu anamuitana, nati, Ndinu wa ku mudzi uti? Ndipo anati, Mnyamata wanu; ndiye wa pfuko tina la Aisrayeli.