7. Ndipo pamene amuna onse a Israyeli okhala m'cigwamo anaona kuti anathawa, ndi kuti Sauli ndi ana ace adafa, anasiya midzi yao, nathawa; nadza Afilisti, nakhala m'menemo.
8. Ndipo m'mawa mwace anafika Afilisti kubvula za ophedwa, napeza Sauli ndi ana ace adagwa pa phiri la Giliboa.
9. Ndipo anambvula natenga mutu wace, ndi zida zace, natumiza ku dziko la Afilisti pozungulirapo, kulalika m'mafano ao ndi mwa anthu.