29. Ndipo Mulungu anampatsa Solomo nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundu mitundu, zonga mcenga uli m'mbali mwa nyanja.
30. Ndipo nzeru ya Solomo inaposa nzeru za anthu onse a kum'mawa, ndi nzeru zonse za ku Aigupto.
31. Pakuti anali wanzeru woposa anthu onse, woposa Etani wa ku Ezra, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Darida ana a Maholi; ndipo mbiri yace inafikira amitundu onse ozungulira.
32. Ndipo ananena miyambo zikwi zitatu, ndipo nyimbo zace zinali cikwi cimodzi mphambu zisanu.