Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yuda 1:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Iwo ndiwo opatukitsa, anthu a makhalidwe acibadwidwe, osakhala naye Mzimu.

20. Koma inu, okondedwa, 3 podzimangirira nokha pa cikhulupiriro canu coyeretsetsa, ndi 4 kupemphera mu Mzimu Woyera,

21. mudzisunge nokha m'cikondi ca Mulungu, ndi 5 kulindira cifundo ca Ambuye wathu Yesu Kristu, kufikira moyo wosatha.

22. Ndipo ena osinkhasinkha muwacitire cifundo,

23. koma ena 6 muwapulumutse ndi kuwakwatula kumoto; koma ena muwacitire cifundo ndi mantha, 7 nimudane naonso maraya ocitidwa mawanga ndi thupi

24. Ndipo 8 kwa iye amene akhoza kukudikirani mungakhumudwe, ndi 9 kukuimikani pamaso pa ulemerero wace opanda cirema m'kukondwera,

25. 10 kwa Mulungu wayekha, Mpulumutsi wathu, mwa Yesu Kristu Ambuye wathu, zikhale ulemerero, ukulu, mphamvu, ndi ulamuliro zisanayambe nthawi, ndi tsopano, ndi kufikira nthawi zonse. Amen.

Werengani mutu wathunthu Yuda 1