Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 9:33-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Ngatiuyu sanacokera kwa Mulungu, sakadakhoza kucita kanthu.

34. Anayankha natikwa iye, Wabadwa iwe konse m'zoipa, ndipo iwe utiphunzitse ife kodi? Ndipo anamtaya kunja.

35. Yesu anamva kuti adamtaya kunja; ndipo pakumpeza iye, anati, Kodi ukhulupirira Mwana wa Mulungu?

36. Iyeyu anayankha nati, Ndipo ndani iye, Ambuye, kuti ndimkhulupirire iye?

37. Yesu anati kwa iye, Wamuona iye, ndiponso wakulankhula ndi iwe ndi Iyeyo.

38. Koma iye anati, Ndikhulupirira, Ambuye; ndipo anamgwadira iye.

39. Ndipo Yesu anati, Kudzaweruza ndadza Ine ku dziko lino lapansi, kuti iwo osapenya apenye; ndi kuti iwo akupenya akhale osaona,

40. Ndipo Afarisi ena akukhala ndi iye anamva izi, nati kwa iye, Kodi ifenso ndife osaona?

41. Yesu anati kwa iwo, Mukadakhala osaona simukadakhala nalo cimo; koma tsopano munena, kuti, Tipenya: cimo lanu likhala.

Werengani mutu wathunthu Yohane 9