Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 9:29-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Tidziwa ife kuti Mulungu analankhula ndi Mose; koma sitidziwa kumene acokera ameneyo,

30. Munthuyu anayankha nati kwa iwo, Pakuti cozizwa ciri m'menemo, kuti inu simudziwa kumene acokera, ndipo ananditsegulira maso anga.

31. Tidziwa kuti Mulungu samvera ocimwa. Koma ngati munthu ali yense akhala wopembedza Mulungu nacita cifuniro cace, amvera ameneyo.

32. Kuyambira paciyambi sikunamveka kuti wina anatsegulira maso munthu wosaona cibadwire.

Werengani mutu wathunthu Yohane 9