Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:55-59 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

55. ndipo 12 inu simunamdziwa iye; koma Ine ndimdziwa iye; ndipo ngati ndinena kuti sindimdziwa iye, ndidzakhala wonama cimodzimodzi inu; koma ndimdziwa iye, ndipo ndisunga mau ace.

56. 13 Atate wanu Abrahamu anakondwera kuona tsiku langa; ndipo anaona, nasangalala.

57. Ayuda pamenepo anati kwa iye, Simunafikire zaka makumi asanu, ndipo munaona Abrahamu kodi?

58. Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, asanayambe kukhala Abrahamu ndipo 14 Ine ndiripo.

59. Pamenepo 15 anatola miyala kuti amponye iye; koma Yesu anabisala, naturuka m'Kacisi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8