Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:40-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Koma tsopano mufuna kundipha Ine, ndine munthu amene ndinalankhula ndi inu coonadi, 3 cimene ndinamva kwa Mulungu; ici Abrahamu sanacita.

41. Inu mucita nchito za atate wanu. Anati kwa iye, Sitinabadwa ife m'cigololo; tiri naye Atate mmodzi ndiye Mulungu.

42. Yesu anati kwa iwo, 4 Mulungu akadakhala Atate wanu, mukadakonda Ine; pakuti Ine ndinaturuka, ndi kucokera kwa Mulungu; pakuti sindinadza kwa Ine ndekha, koma Iyeyu anandituma Ine.

43. Simuzindikira malankhulidwe anga cifukwa ninji? Cifukwa simungathe kumva mau anga,

44. 5 Inu muli ocokera mwa atate wanu mdierekezi, ndipo zolakalaka zace za atate wanu mufuna kucita. Iyeyu anali wambanda kuyambira paciyambi, ndipo sanaima m'coonadi, pakuti mwa iye mulibe coonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wace; pakuti ali wabodza, ndi atate wace wa bodza.

45. Koma Ine, cifukwa ndinena coonadi, simukhulupirira Ine.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8