Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:33-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Anamyankha iye, Tiri mbeu ya Abrahamu, ndipo sitinakhala akapolo a munthu nthawi iri yonse; munena bwanji; Mudzayesedwa aufulu?

34. Yesu anayankha iwo, nati, Indetu, indetu, ndinena kwa inu kuti yense wakucita cimo ali kapolo wa cimolo.

35. Koma kapolo sakhala m'nyumba nthawi yonse; mwana ndiye akhala nthawi yonse.

36. Cifukwa cace ngati Mwana adzakuyesani inu aufulu, mudzakhala mfulu ndithu.

37. Ndidziwa kuti muli mbeu ya Abrahamuj koma mufuna kundipha Ine, cifukwa mau anga alibe malo mwa inu.

38. 1 Zimene ndinaona Ine kwa Atate, ndilankhula; ndipo inunso mucita cimene mudamva kwa atate wanu.

39. Anayankha nati kwa iye, Atate wathu ndiye Abrahamu. Yesu ananena nao, 2 Ngati muli ana a Abrahamu, mukadacita nchito za Abrahamu.

40. Koma tsopano mufuna kundipha Ine, ndine munthu amene ndinalankhula ndi inu coonadi, 3 cimene ndinamva kwa Mulungu; ici Abrahamu sanacita.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8