Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Koma alembi ndi Afarisi anabwera naye kwa iye mkazi wogwidwa m'cigololo, ndipo pamene anamuimika iye pakati,

4. ananena kwa iye, Mphunzitsi, mkazi uyu wagwidwa alimkucita cigololo.

5. Koma m'cilamulo Mose anatilamulira, ttwaponye miyala otere. Cifukwa cace Inu munena ciani za iye?

6. Koma ici ananena kuti amuyese iye, kuti akhale naco comneneza iye. Koma Yesu, m'mene adawerama pansi analemba pansi ndi cala cace.

7. Koma pamene anakhalakhala alikumfunsabe iye, anaweramuka, nati kwa iwo, Amene mwa inu ali wopanda cimo, ayambe kumponya mwala,

8. Ndipo m'mene adaweramanso analemba ndi cala cace pansi.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8