Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 8:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Mau awa analankhula m'nyumba ya cuma ca Mulungu pophunzitsa m'Kacisi; ndipo palibe munthu anamgwira iye, pakuti nthawi yace siinafike.

21. Pamenepo anatinso kwa iwo; Ndimuka Ine, ndipo mudzandifuna, ndipo m'cimo lanu mudzafa: kumene ndimukako Ine, simudziwa kudza inu.

22. Cifukwa cace Ayuda ananena, Kodi adzadzipha yekha, pakuti ananena, Kumene ndimukako Ine, simudziwa inu kudza?

23. Ndipo ananena nao, Inu ndinu ocokera pansi; Ine ndine wocokera Kumwamba; inu ndinu a dziko lino lapansi; sindiri Ine wa dziko lino lapansi.

24. Cifukwa cace ndinati kwa inu, kuti mudzafam'macimo anu, pakuti ngati simukhulupirira kuti Ine ndine, mudzafa m'macimo anu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 8