Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:39-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Koma 1 ici anati za Mzimu, amene iwo akukhulupirira iye anati adzalandire; pakuti Mzimu panalibe pamenepo, cifukwa Yesu sanalemekezedwa panthawi pomwepo.

40. Pamenepo ena a khamulo pakumva mau awa, ananena, 2 Mnene riyo ndi uyu ndithu.

41. Ena ananena, 3 Uyu ndi Kristu, Koma ena ananena, Kodi Kristu adza kuturuka m'Galileya?

42. 4 Kodi sicinati cilembo kuti Kristu adza kuturuka mwa mbeu ya Davine, ndi kucokera ku Betelehemu, kumudzi kumene kunali Davine?

43. 5 Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo cifukwa ca iye.

Werengani mutu wathunthu Yohane 7