Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:37-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Koma tsiku lomariza, lalikurulo la phwando, Yesu anaimirira napfuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva Ludzu, adze kwa Ine, namwe.

38. Iye wokhulupirira Ine, monga cilembo cinati, Mitsinje ya madzi amoyo idzayenda, kuturuka m'kati mwace.

39. Koma 1 ici anati za Mzimu, amene iwo akukhulupirira iye anati adzalandire; pakuti Mzimu panalibe pamenepo, cifukwa Yesu sanalemekezedwa panthawi pomwepo.

40. Pamenepo ena a khamulo pakumva mau awa, ananena, 2 Mnene riyo ndi uyu ndithu.

41. Ena ananena, 3 Uyu ndi Kristu, Koma ena ananena, Kodi Kristu adza kuturuka m'Galileya?

42. 4 Kodi sicinati cilembo kuti Kristu adza kuturuka mwa mbeu ya Davine, ndi kucokera ku Betelehemu, kumudzi kumene kunali Davine?

43. 5 Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo cifukwa ca iye.

44. Koma 6 ena mwa iwo anafuna kumgwira iye; koma palibe munthu anamgwira kumanja.

45. Pamenepo anyamatawo anadza kwa ansembe akulu ndi Afarisi; ndipo iwowa anati kwa iwo, Simunamtenga iye bwanji?

46. Anyamatawo anayankha, 7 Nthawi yonse palibe munthu analankhula cotero.

47. Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?

48. 8 Kodi wina wa akuru anakhulupirira iye, kapena wa Afarisi?

49. Koma khamu ili losadziwa cilamulo, likhala lotembereredwa.

50. 9 Nikodemo ananena kwa iwo, amene uja adadza kwa iye kale, ali mmodzi wa iwo,

Werengani mutu wathunthu Yohane 7