Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 7:32-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Afarisi anamva khamu la anthu ling'ung'udza zimenezi za iye; ndipo ansembe akulu ndi Afarisi anatuma anyamata kuti akamgwire iye.

33. Pamenepo Yesu anati, Katsala kanthawi ndiri ndi inu, ndipo ndimuka kwa iye wondituma Ine.

34. Mudzafunafuna Ine, osandipeza; ndipo pomwe ndiri Ine, inu simungathe kudzapo.

35. Cifukwa cace Ayuda anati mwa iwo okha, Adzanka kuti uyu kuti ife sitikampeza iye? kodi adzamuka kwa Ahelene obalalikawo, ndi kuphunzitsa Ahelene?

36. Mau awa amene ananena ndi ciani, Mudzandifunafuna osandipeza Ine: ndipo pomwe ndiri Ine, inu simungathe kudzapo?

37. Koma tsiku lomariza, lalikurulo la phwando, Yesu anaimirira napfuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva Ludzu, adze kwa Ine, namwe.

38. Iye wokhulupirira Ine, monga cilembo cinati, Mitsinje ya madzi amoyo idzayenda, kuturuka m'kati mwace.

39. Koma 1 ici anati za Mzimu, amene iwo akukhulupirira iye anati adzalandire; pakuti Mzimu panalibe pamenepo, cifukwa Yesu sanalemekezedwa panthawi pomwepo.

40. Pamenepo ena a khamulo pakumva mau awa, ananena, 2 Mnene riyo ndi uyu ndithu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 7