Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 6:38-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Pakuti ndinatsika Kumwamba, si kuti ndicite cifuniro canga, koma cifuniro ca iye amene anandituma Ine.

39. Koma cifuniro ca Iye amene anandituma Ine ndi ici, kuti za ici conse Iye anandipatsa Ine ndisatayeko kanthu, koma ndiciukitse tsiku lomariza.

40. Pakuti cifuniro ca Atate wanga ndi ici, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.

41. Cifukwa cace Ayuda anang'ung'udza za iye, cifukwa anati, Ine ndine mkate wotsika Kumwamba.

42. Ndipo iwo ananena, Si Yesu uyu, mwana wa Yosefe, atate wace ndi amai wace tiwadziwa? Anena bwanji tsopano, kuti, Ndinatsika Kumwamba?

43. Yesu anayankha nati kwa iwo, Musang'ung'udze winandi mnzace.

Werengani mutu wathunthu Yohane 6