Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 6:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. ndipo pamene adalowa m'ngalawa, analikuoloka nyanja kunka ku Kapernao. Ndipo kutada pamenepo, koma Yesu asanadze kwa iwo.

18. Ndipo nyanja inalikuuka cifukwa ca mphepo yaikulu yakuombako.

19. Ndipo parnene adapalasa monga mastadiya makumi awiri ndi asanu kapena makumi atatu, anaona Yesu alikuyenda panyanja, ndi kuyandikira ngalawa; ndipo anacita mantha.

20. Koma iye ananena nao, ndine; musaope.

21. Pamenepo analola kumlandira m'ngalawa; ndipo pomwepo ngalawayo inafika kumtunda kumene analikunkako.

22. M'mawa mwace khamu la anthu limene linaima tsidya lija la nyanja linaona kuti palibe ngalawa yina koma imodzi, ndi kuti Yesu sanalowa pamodzi ndi akuphunzira ace m'ngalawamo, koma akuphunzira ace adacoka pa okha;

Werengani mutu wathunthu Yohane 6