Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 6:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitapita izi anacoka Yesu kunka ku tsidya lija la nyanja ya Galileya, ndiyo ya Tiberiya,

2. Ndipo khamu lalikuru la anthu linamtsata iye, cifukwa anaona zizindikilo zimene anacita pa odwala.

3. Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.

4. Ndipo Paskha, phwando la Ayuda, anayandikira.

5. Pamenepo Yesu, pokweza maso ace, ndi kuona kuti khamu lalikuru lirinkudza kwa iye, ananena kwa Filipo, Tidzagula kuti mikate kuti adye awa?

6. Koma ananena ici kuti amuyese; pakuti anadziwa yekha cimene adzacita.

Werengani mutu wathunthu Yohane 6