39. 2 Musanthula m'malembo, popeza muyesa kuti momwemo muli nao moyo wosatha; ndipo akundicitira Ine umboni ndi iwo omwewo;
40. ndipo 3 simufuna kudza kwa Ine, kuti mukhale nao moyo.
41. 4 Ulemu sindiulandira kwa anthu.
42. Koma ndikudziwani inu, kuti mulibe cikondiea Mulungu mwa inu nokha.
43. Ndadza Ine m'dzina la Atate wanga, ndipo simundilandira Ine; akadza wina m'dzina lace la iye mwini, iyeyu mudzamlandira.
44. Mungathe inu bwanji kukhulupira, 5 popeza mulandira ulemu wina kwa mnzace ndipo ulemu wakucokera kwa Mulungu yekha simuufuna?
45. Musayesa kuti Ine ndidzakunenezani inu kwa Atate; 6 pali wakukunenezani, ndiye Mose, amene inu mumtama.
46. Pakuti mukadakhulupirira Mose, mukadakhulupirira Ine; 7 pakuti iyeyu analembera za Ine.
47. Koma ngati simukhulupirira malembo a iyeyu, mudzakhulupirira bwanji mau anga?