Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 5:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitapita izi panali phwando la Ayuda; ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.

2. Koma pali thamanda m'Yerusalemu pa cipata ca nkhosa, lochedwa m'Cihebri Betesda, liri ndi makumbi asanu.

3. M'menemo munagona khamu lalikuru la anthu odwala akhungu, opunduka miyendo, opuwala. [

4. ]

5. Koma panali munthu wina apo, ali m'kudwala kwace zaka makumi atatu kudza zisanu ndi zitatu.

Werengani mutu wathunthu Yohane 5