Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pakuti ophunzira ace adacoka kunka kumudzi kuti akagule cakudya.

9. Pamenepo mkazi wa m'Samariya ananena ndi iye, Bwanji Inu, muli Myuda, mupempha kwa ine kumwa, ndine mkazi Msamariya? (pakuti Ayuda sayenderana nao Asamariya),

10. Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.

11. Mkaziyo ananena ndi Iye, Ambuye, mulibe cotungira madzi, ndi citsime ciri cakuya; ndipo mwatenga kuti madzi amoyo?

12. kodi muli wamkuru ndi atate wathu Yakobo amene anatipatsa ife citsimeci, namwamo iye yekha, ndi ana ace, ndi zoweta zace?

Werengani mutu wathunthu Yohane 4