Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Cifukwa cace anadza ku mudzi wa Samariya, dzina lace Sukari, pafupi pa kadziko kamene Yakobo adapatsa mwana wace Yosefe;

6. ndipo pamenepo panali citsime ca Yakobo. Ndipo Yesu, popeza analema ndi ulendo wace, motero anakhala pacitsime,

7. Kunali ngati ora lacisanu ndi cimodzi. Kunadza mkazi woturuka m'Samariya kudzatunga madzi. Yesu ananena naye, Undipatse Ine ndimwe.

8. Pakuti ophunzira ace adacoka kunka kumudzi kuti akagule cakudya.

9. Pamenepo mkazi wa m'Samariya ananena ndi iye, Bwanji Inu, muli Myuda, mupempha kwa ine kumwa, ndine mkazi Msamariya? (pakuti Ayuda sayenderana nao Asamariya),

10. Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.

Werengani mutu wathunthu Yohane 4