Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 4:48-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

48. Pamenepo Yesu anati kwa iye, Ngati simuona zizindikilo ndi zozizwa, simudzakhulupira.

49. Mkuluyo ananena kwa iye, Ambuye, tsikani asanafe mwana wanga.

50. Yesu ananena naye, Muka, mwana wako ali ndi moyo, Munthuyo anakhulupirira mau amene Yesu anatero naye, namuka.

51. Ndipo m'mene analikutsika, akapolo ace anakomana, naye, nanena, kuti, Mwana wanu ali ndi moyo.

52. Cifukwa cace anawafunsa ora lace anayamba kuciralo. Pamenepo anati kwa iye, kuti, Dzulo, ora lacisanu ndi ciwiri malungo anamsiya.

53. Cifukwa cace atateyo anadziwa kuti ndi ora lomwelo limene Yesu anati kwa iye, Mwana wako ali ndi moyo; ndipo anakhulupira iye yekha ndi a pa banja lace onse.

Werengani mutu wathunthu Yohane 4